Home Politics Phungu Wopanda Chipani Alingati Maliro Opanda Mpingo

Phungu Wopanda Chipani Alingati Maliro Opanda Mpingo

by Aubrey Kausiwa
0 comments

Mlembi wa mkulu wa chipani cha Malawi Congress yemwenso ndi nduna ya maboma ang’ono ang’ono, umodzi ndi chikhalidwe a Richard Chimwendo Banda afanizila aphungu oima pa okha ngati maliro opanda mpingo.

Iwo alankhula izi pa bwalo la zamasewero la Gawamadzi mfumu yaikulu Chiwere pa msonkhano wa ndale m’boma la Dowa.

A Chimwendo ati ndikovuta kukhulupilira munthu yemwe alibe chipani ponena kuti ali ndikuthekera kodzawathawa anthu akadzapambana chisankho.

Iwo apempha anthu m’bomali kuti asadzachite chibwana kusankha munthu yemwe siwachipani cha MCP koma adzasankhe a Martin Luka kamba koti ndi munthu wa khalidwe.

Pa Msonkhanowu phungu yemwe akuimila chipani cha MCP m’dera la pakati kum’mawa kwa boma la Dowa a Martin Luka akhazikitsa mpikisano wa masewero a mpira wa ndalama zokwana K2 million.

You may also like

Leave a Comment

Yetu community radio was established in 2018 by the United Nations High Commissioner for Refugees (UNHCR) with the mission of serving as a model of peaceful co-existence between the Malawian and refugee communities in addressing issues of child protection, GBV, and human rights by providing a platform for all people to access information and speak on issues that affect them through media programming. Yetu community radio boasts of being a unique radio as it is based in a refugee camp setup and is the only radio in Malawi that broadcasts in five languages, namely; English, Chichewa, Kiswahili, French, and Kinyarwanda. The station broadcasts on 107.6 MHZ across the central region of Malawi.

Newsletter

@2025 – All Right Reserved. MACRA Community Radios

Are you sure want to unlock this post?
Unlock left : 0
Are you sure want to cancel subscription?
-
00:00
00:00
Update Required Flash plugin
-
00:00
00:00