Home Business Kusintha Ulimi Kukhala Malonda

Kusintha Ulimi Kukhala Malonda

by Aubrey Kausiwa
0 comments

Nduna ya zaulimi a Sam Dalitso Kawale ati ndi okhutira ndi momwe ntchito ya ulimi wa minda ikukuikulu (Mega Farm) ikuyendera m’boma la Dowa.

A Kawale alankhula izi atamaliza kuyendera minda ikukuikulu ya Lonjezo komanso Bowe EPA ku Mponela m’bomali.

Polankhula ndi wailesi ya Yetu, a Kawale ati ntchito yomwe alimi akuluakulu akugwira m’bomali ikugwirizana ndi masomphenya a boma opanga ulimi kukhala malonda.

A Kawale anaonjeranso kuti chimangachi chithandiziranso maanja a m’bomali kukhala odzidalira pa chakudya.

Kumbali yake, m’modzi mwa alimi omwe amayang’anira munda wa Lonjezo womwe ndi wa mahekitala okwana 82, a Gift Kadam’manja, athokoza boma kamba ka thandizo la zipangizo za ulimi.

A Kadamanja ati akolola matumba achimanga oposera 8000 zomwe paokha sakanakwanitsa.

Pomwe a Wilson Zimba ochokera ku Bowe EPA m’mudzi mwa Chakhadza akuyembekezera kukolora matumba a chimanga opitilira 10,000 pamunda wa mahekitala okwana 112.

You may also like

Leave a Comment

Yetu community radio was established in 2018 by the United Nations High Commissioner for Refugees (UNHCR) with the mission of serving as a model of peaceful co-existence between the Malawian and refugee communities in addressing issues of child protection, GBV, and human rights by providing a platform for all people to access information and speak on issues that affect them through media programming. Yetu community radio boasts of being a unique radio as it is based in a refugee camp setup and is the only radio in Malawi that broadcasts in five languages, namely; English, Chichewa, Kiswahili, French, and Kinyarwanda. The station broadcasts on 107.6 MHZ across the central region of Malawi.

Newsletter

@2025 – All Right Reserved. MACRA Community Radios

Are you sure want to unlock this post?
Unlock left : 0
Are you sure want to cancel subscription?
-
00:00
00:00
Update Required Flash plugin
-
00:00
00:00